The Cichlid Fishes of Lake Malawi, Africa
 

Abstract of Publication

Arnegard, M.E., and J. Snoeks. 2001. New three-spotted cichlid species with hypertrophied lips (Teleostei: Cichlidae) from the deep waters of Lake Malawi/Nyasa, Africa. Copeia 2001 (3): 705-717.  

GANIZO LENILENI MWA CHIDULE (Chichewa Abstract; translated by Dalitso Richard Kafumbata)

Kufikira lero, pali mitundu ya nsomba za m'gulu la mbuna, chisawasawa, ndunduma, utaka, ncheni, gundamwala, kabibi ndi zina zotero yokwana pafupifupi mazana atatu ndi mphambu makumi atatu yomwe ili yodziwika bwinobwino. Nsomba zimenezi zimapezeka mu nyanja ya Malawi yokha muno mu Africa ndi pa dziko lonse lapansi. Komabe pali mitundu ya nsomba zomwezi yochuluka kwambiri yomwe sinadziwike kwenikweni. Pano ndikufuna kufotokoza za nsomba ina ya tsopano ya m'gulu lomweli yomwe imapezeka m'malo akuya mu nyanja ya Malawi. Nsombayi ndaiphatika mu mtundu wotchedwa Otopharynx. Nsombayi ili ndi madontho atatu mnthiti mwake ndi mano okhuthala okhala ndii nsonga ziwiri. Nsombayi ndi yokulupala ndipo ikusiyana ndi nsomba zina za madontho atatu zopezekanso m'gululi chifukwa cha mlomo wake womwe ndi wochindikala wangowe. Mlomo woterewu ungagwiritsidwe ntchito ngati lilime pomvera kakomedwe ndi kawawidwe ka chakudya. Ndifotokozanso za khalidwe ndi maonekedwe ena a nsombayi omwe akuyisiyanitsa ndi nsomba zinzake za m'gululi. Makhazikitsidwe a khalidwe ndi maonekedwe a nsomba za m'gulu la Otopharynx amasiyana ndi nsomba zina zonse za m'gulu la mbuna, chisawasawa, ndunduma, utaka, ncheni, gundamwala, kabibi ndi zina zotero. Pa chifukwa ichi gulu limeneli likuoneka ngati ndiloima palokha. Ngakhale izi zili chonchi, gulu limeneli ndilovomerezeka pakali pano ndipo likuthandiza pa chintchito choika nsomba zooneka zofananafanana m'makhalidwe ndi m'maonekedwe m'magulu osiyana.
 

 

 

 

free hit counters